Chida cha Mphamvu ya Mulungu, Pemphero
Ophunzira Anazindikira Mmene
Angavekedwe ndi Mphamvu ya
Mulungu Kupyolera Mtsiku Lokwera Kumwamba
Ophunzira, amene anaona Yesu akukwera kuchokera
ku Phiri la Azitona, anazindikira kuti popanda
kuvala mzimu woyera wa Mulungu, Uthenga
Wabwino sungalalikidwe padziko lonse lapansi.
Chotero, iwo anapemphera mowona mtima kwa
masiku khumi kuchokera pa Tsiku la Kukwera
Kumwamba kufikira pa Tsiku la Pentekoste,
kupempha Mzimu Woyera wa mvula yoyambayo.
N’chifukwa Chiyani Akhristu a Mpingo wa
Mulungu Amapemphera Modzipereka
Kuyambira pa Tsiku la Kukwera
Kumwamba Kufikira pa Tsiku la Pentekosite?
Pamene Eliya anagonjetsa aneneri
onyenga 850 pa Phiri la Karimeli,
pemphero linatsogolera chipambanocho.
Yesu, Khristu Ahnsahnghong, ndi Mulungu Amayi,
amene anabwera padziko lino lapansi kudzapulumutsa
anthu, anapereka chitsanzo poyamba ntchito
Yawo ya uthenga wabwino ndi mapemphero
a m’bandakucha tsiku lililonse.
Choncho, mamembala a Mpingo wa
Mulungu, nawonso, amayamba tsiku
lawo, kupeza mphamvu zauzimu
kudzera mu pemphero.
Pemphani, ndipo chidzapatsidwa kwa
inu; funani, ndipo mudzapeza; gogodani,
ndipo chidzatsegulidwa kwa inu;
Pakuti yense wakupempha alandira;
ndi wofunayo apeza; ndi iye
amene agogoda adzamtsegulira.
Mateyu 7:7-8
Chifukwa chake ndinena ndi inu,
Zinthu zilizonse mukazipemphera
ndi kuzipempha, khulupirirani kuti
mwazilandira, ndipo mudzakhala nazo.
Marko 11:24
Nambala ya Owonera32
#Madyelero
#Chiyembekezo
#Pemphero