N
Gehena
Gehena ndi malo owopsa kwambiri,
kumene ndikovuta kulandira angakhale
dontho la madzi pamene uli m'mazunzo a moto.
(Luka 16:24)
Yesu anati ngati dzanja lathu, phazi, kapena diso
litichimwitsa, ndi bwino kulidula kapena
kulikolowola, kusiyana ndi kupita ku gehena.
(Marko 9:43)
Ndichifukwa chakuti mazunzo a gehena
sangayerekezedwe ndi ululu wodula
chiwalo cha thupi lathu.
"Kumene mphutsi yawo siifa,
ndi moto suzima ku gehena." (Marko 9:48)
“Pakuti onse adzathiridwa mchere wamoto” (Marko 9:49)
Ngakhale chilango cha gehena ndi
chopweteka kwambiri, sitingathe kufa mwatokha.
Ku gehena, kulibe chisangalalo cha moyo,
kulibe mpumulo, kapena chiyembekezo cha
chipulumutso, koma ululu, madandaulo ndi chisoni chokha.
Chifukwa chiyani timapita ku gehena
ngati sitilapa titamva uthenga wabwino?
Tisanabadwe padziko lapansi,
tinali angelokumwamba.
(Yobu 38:4–21)
Komabe, tinachimwa kumwamba
ndikulandira chilango chopita ku gehena.
Choncho tinabadwa pa dziko,ndende yauzimu,
ndipo tili kuno moyembekedzera.
(Ezekiele28:13–17)
Ngati sitifunafuna njira yopewera chilango cha
gehena padziko lino, tsogolo lathu ndilopita ku gehena latsimikizidwa.
“Munthu wosauka ine;
adzandilanditsa ndani m'thupi la imfa iyi?”
(Aroma 7:24)
Mulungu anachitira chifundo
anthu omwe anayenera kulandira chilango cha gehena,
ndipo Iye Mwini anabwera padziko kusonyeza
njira yopewera chilango cha gehena.
“Ndadza kudzaitana ochimwa kuti alape.” (Luka 5:32)
Kuti atikhululukire machimo athu
otsogolera kuimfa ndi kutipulumutsa
ku chilango cha gehena, Mulungu anapereka
thupi ndi mwazi Wake ngati dipopa anthu, ochimwa.
“Tengani, idyani; mkate wa
Paska ndi thupi langa.” (Mateyu 26:26)
“Vinyo wa Paska ndi mwazi Wanga
wa pangano, wothiridwa chifukwa cha
anthu ambiri ku kuchotsa machimo.” (Mateyu 26:28)
Tikasunga Paska wa pangano latsopano,
timadalitsidwa ndi chikhululukiro cha machimo
ndi kupulumutsidwa ku chilango cha gehena.
Ndiponso, tikhoza kulandira
moyo wosatha ndikubwerera kumwamba.
“Iyewakudya thupi langa ndi kumwa
mwazi wanga ali nao moyo wosatha,
ndipo Ine ndidzamuukitsa iye tsiku lomaliza.”
(Yohane 6:54)
Komabe, ngati tikana uthenga wakuti,
“Landirani chikhululukiro cha machimo
ndi moyo wosatha kudzera mu Paska,”
machimo amene tinachita kumwamba
sangakhululukidwe, ndipo tidzalandira
chilango cha gehena monga momwe zinakonzedwera.
“Ndinalakalaka ndithu kudya
Paska uwu pamodzi ndinu
ndisanayambe kusautsidwa.”
(Luka 22:15)
Chonde sungani Paska wa pangano
latsopano, chizindikiro cha Mulungu pa chikhululukiro
cha machimo, ndikubwerera kumwamba!
Nambala ya Owonera8
#TUBE