Zamoyo zonse zimalandira moyo kudzera mwa amai awo. Kaya cholengedwacho ndi chaching'ono bwanji, amayi ali ndi chikondi chodzipereka cha amai chomwe chimawalora kupereka moyo wawo chifukwa cha ana awo. N’chifukwa chiyani Mulungu analenga zinthu zonse kuti zilandire moyo kudzera mwa amai awo? Ndipo n’chifukwa chiyani amai, ngakhale amai a zolengedwa zazing'ono, onse ali ndi chikondi cha amai? Mulungu, amene analenga zinthu zonse mwa chifuniro Chake, anatiululira njira yolandirira moyo wosatha, kudzera mu mfundo yobadwa pa dziko lino komanso khalidwe labwino la Mulungu Amai. Zamoyo zonse zimakhala ndi utali wamoyo umene zinalandira kwa amai awo. Choncho, tingalandire moyo wosatha kudzera mwa Amai athu auzimu. Zili choncho chifukwa Mulungu Amai okha, omwe ali ndi moyo wosatha, angatipatse moyo wosatha. Mu m’badwo uno, tiyenera kukhala ana a Mulungu Amai kuti tilandire moyo wosatha. Bwerani ku Mpingo wa Mulungu womwe umakhulupirira mwa Mulungu Amai!
119 Bundang P.O.Box, Bundang-gu, Seongnam-si, Gyeonggi-do, Rep. of KOREA
Tel 031-738-5999 Fax 031-738-5998
Likulu la Ofesi: 50, Sunae-ro, Bundang-gu, Seongnam-si, Gyeonggi-do, Dziko la Korea
Mpingo Waukulu: 35, Pangyoyeok-ro, Bundang-gu, Seongnam-si, Gyeonggi-do, Dziko la Korea
ⓒ Gulu la Utumiki wa Dziko Lonse la Mpingo wa Mulungu. Ma Umwini onse ndi Otetezedwa Mfundo za Zinsinsi