Titha kuona mphamvu ya mawu a Mulungu pamene Adamu ndi Hava anafa pakudya zipatso za mtengo wakudziwitsa zabwino ndi zoipa; wachifwamba wa kudzanja lamanja pa mtanda anapulumutsidwa; akhungu awiriwo anachiritsidwa; mkaziyo amene amataya magazi kwa zaka khumi ndi ziwiri, anachiritsidwa; ndipo kudzera zenizenizake yense wakudya thupi la Yesu ndi kumwa mwazi wake pa kutengapo mbali pa Paskha mkate ndi vinyo adzalandira mphatso ya moyo wosatha.
M’nthawi ya Mwana, Yesu yekha anapatsa madzi amoyo kwa anthu amene anabwera kwa Iye pa Tsiku Lomaliza ndi Lalikulu Kwambiri la Phwando la Misasa.
Mu m'badwo wa Mzimu Woyera, iwo amene amabwera kwa Khristu Ahnsahnghong ndi Mulungu Amayi, amene anabwera ngati Mzimu ndi Mkwatibwi, adzalandira madzi a moyo, umenewo ndi Mzimu Woyera. Ndiwo amene angathe kukwaniritsa zinthu zonse ndi mphamvu ya mawu a Mulungu.
Koma tsiku lomaliza, lalikululo la chikondwerero, Yesu anaimirira nafuula, ndi kunena, Ngati pali munthu akumva ludzu, adze kwa Ine, namwe.4 Iye wokhulupirira Ine, monga chilembo chinati, Mitsinje ya madzi amoyo idzayenda, kutuluka m'kati mwake. Koma ichi anati za Mzimu, amene iwo akukhulupirira Iye anati adzalandire;...
Yohane 7:37-39
Ndipo Mzimu ndi mkwatibwi anena, Idzani. Ndipo wakumva anene, Idzani. Ndipo wakumva ludzu adze; iye wofuna, atenge madzi a moyo kwaulere.
Chivumbulutso 22:17
119 Bundang P.O.Box, Bundang-gu, Seongnam-si, Gyeonggi-do, Rep. of KOREA
Tel 031-738-5999 Fax 031-738-5998
Likulu la Ofesi: 50, Sunae-ro, Bundang-gu, Seongnam-si, Gyeonggi-do, Dziko la Korea
Mpingo Waukulu: 35, Pangyoyeok-ro, Bundang-gu, Seongnam-si, Gyeonggi-do, Dziko la Korea
ⓒ Gulu la Utumiki wa Dziko Lonse la Mpingo wa Mulungu. Ma Umwini onse ndi Otetezedwa Mfundo za Zinsinsi